Marko 16:16

Iye amene akhulupirira nabatizidwa adzapulumutsidwa; koma iye amene sakhulupirira adzawonongedwa.


Machitidwe 2:38

Ndiye Petro anati kwa iwo, Lapani, ndipo mubatizidwe wina aliyense wa inu mu dzina la Yesu Khristu Kwa chikhululukiro cha machimo, ndipo inu mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.



Ndi chachidziwikireni, kuti ubatizo ndi wofunika kwambiri, koma kodi ziri ndi kanthu kuti tabatizidwa chotani? Kodi ulipo ubatizo wolondola, kapena kodi chirichonse chingagwire ntchito? Ngati inu mumakhulupirira Baibulo, ndiye INDE, ulipo ubatizo wolondola.

Mipingo yambiri imabatiza mu Dzina la Atate, Mwana, ndi Mzimu Woyera, koma izi sizolondola monga mwa Baibulo.

Mu Machitidwe 19, panali anthu ena amene anali atamukhulupirira kale Yesu Khristu, koma anali asanalandirebe Mzimu Woyera mmitima mwawo. Mtumwi Paulo ankadziwa njira yolondola yoti alandirire Mzimu Woyera, kotero iye anawafunsa iwo, “Kodi inu munabatizidwa mu chiyani?” Ndipo iwo anati, “Mu ubatizo wa Yohane.” (Machitidwe 19:3) Paulo anawona kuti iwo anali asanabatizidwe molingana ndi kulamula kwa Petro mu Machitidwe 2:38, kotero iye anawalangiza iwo kuti abatizidwenso mu Dzina la Ambuye Yesu. Kenako, monga zinalonjezedwa, iwo analandira Mzimu Woyera.

Chotero, ndi chifukwa chiyani ophunzira ankabatiza mu Dzina la Yesu pamene Yesu, Mwiniwake, anawauza iwo kuti azibatiza mu Dzina (osati “mmaina”) la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera? (Mateyu 28:19) Kodi iwo analakwitsa? Ayi! Iwo anachita ndendende monga iwo analangizidwa.

Pamene inu mukuwerenga nkhani iyi, muganizire za dzina lanu. Kodi ndinu mwana? Kodi dzina lanu ndi, “Mwana”? Kodi ndinu mayi? Kodi dzina lanu ndi, “Mayi”? Ndithudi ayi, amenewo ndi maudindo chabe. Inu muli nalo dzina lenileni, chomwechonso Mulungu.

Yankho lake ndi ili:

Ndipo mulibe chinthu choterocho mu Baibulo monga aliyense kukhala atabatizidwapo mu dzina la Atate, Mwana, Mzimu Woyera; chifukwa palibe chinthu choterocho. Atate si dzina; ndipo Mwana si dzina; ndi Mzimu Woyera si dzina, koma Dzina la Atate, Mwana, Mzimu Woyera ndi Ambuye Yesu Khristu.

Yesu Khristu ndi Mulungu! Iyeyo ndi Atate, Mwana, ndi Mzimu Woyera.

Ngati inu mukufunafuna Mzimu Woyera ndipo mukudabwa kuti chifukwa chiyani Ambuye sanakupatsenibe inu iwo, ndiye inu mukhoza kufuna kudzifunsa nokha funso lomwelo limene Paulo anafunsa, “Ndiye kodi inu munabatizidwa mu chiyani?”


Zothandizira zake

Mateyu 28:19

Pitani inu chotero, ndipo mukawaphunzitse mafuko onse, kukawabatiza iwo mu Dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera:

[Kodi Dzina la Atate ndi liti? Dzina la Mwana? Dzina la Mzimu Woyera?]

Marko 16:16

Iye amene akhulupirira ndipo nabatizidwa adzapulumutsidwa; koma iye amene sakhulupirira adzawonongedwa.

Yohane 5:43

Ine ndinabwera mu dzina la Atate anga, ndipo inu simunandilandire ine: ngati wina adzabwera mu dzina lake lake, ameneyo inu mudzamulandira.

[Ngati Iye anabwera mu Dzina la Atate Ake, ndiye Dzina lakelo ndi liti?]

Yohane 10:30

Ine ndi Atate anga ndife mmodzi

Yohane 12:45

Ndipo iye amene wandiwona ine wamuwona iye amene anandituma ine.

Yohane 14:8-9

Fillipo ananena ndi iye, Ambuye, tiwonetsereni ife Atate, ndipo chitikwanira ife.

Yesu ananena kwa iye, Ine ndakhala ndi inu nthawi yonseyi, ndipo mpaka pano inu simukundidziwabe ine, Fillipo? iye amene wandiwona ine wawawona Atate, ndipo iwe ukuneneranji ndiye, Mutiwonetse ife Atate?

Yohane 20:27-28

Pomwepo ananena iye kwa Tomasi, Bwera nacho chala chako kuno; nuwone manja anga; ndipo bwera nalo dzanja lako, nuliike ku nthiti yanga: ndipo usakhale wosakhulupirira, koma wokhulupirira.

Ndipo Tomasi anayankha nati kwa iye, Ambuye wanga ndi Mulungu wanga.

Machitidwe 2:38-39

Ndipo Petro anati kwa iwo, Lapani, ndipo mubatizidwe yense wa inu mu dzina la Yesu Khristu kuloza ku chikhululukiro cha machimo anu, ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.

Pakuti lonjezano liri kwa inu, ndi kwa ana anu, ndi kwa onse akutali, onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawaitana.

Machitidwe 4:12

Palibepo chipulumutso mwa wina aliyense: pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo la kumwamba lopatsidwa mwa anthu, limene tiyenera kupulumutsidwa nalo.

Machitidwe 8:12

Koma pamene anakhulupirira Filipo akulalikira zinthu za ufumu wa Mulungu, ndi dzina la Yesu Khristu, iwo anabatizidwa, amuna ndi akazi.

Machitidwe 19:3-6

Ndipo iye anati kwa iwo, Nanga munabatizidwa mu chiyani? Ndipo iwo anati, Mu ubatizo wa Yohane.

Ndiye anati Paulo, Yohane ndithudi anabatiza ndi ubatizo wa kutembenuka mtima, nati kwa anthu, kuti amkhulupirire iye amene adzaza pambuyo pache, ndiye, pa Khristu Yesu.

Pamene iwo anamva ichi, iwo anabatizidwa mu dzina la Ambuye Yesu.

Ndipo pamene Paulo anaika manja ake pa iwo, Mzimu Woyera anadza pa iwo; ndipo iwo analankhula ndi malirime, ndipo ananenera.

Aefeso 4:5

Ambuye mmodzi, chikhulupiriro chimodzi, ubatizo umodzi.

Akolose 3:17

Ndipo chirichonse chimene inu muchichita mu mawu kapena mu ntchito, muzichita zonse mu dzina la Ambuye Yesu, ndi kuyamika Mulungu Atate mwa iye.

I Yohane 5:7

Pakuti alipo atatu amene amachitira umboni kumwamba, Atate, Mawu, ndi Mzimu Woyera: ndipo atatu awa ndi mmodzi.